Yobu 33:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,

9. Ndine woyera ine, wopanda kulakwa,Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.

10. Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;

11. Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.

Yobu 33