8. Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,
9. Ndine woyera ine, wopanda kulakwa,Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.
10. Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;
11. Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.