Yobu 33:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Mnofu wace udatha, kuti sungapenyeke;Ndi mafupa ace akusaoneka aturuka.

22. Inde wasendera kufupi ku manda,Ndi moyo wace kwa akuononga.

23. Akakhala kwa iye mthenga,Womasulira mau mmodzi mwa cikwi,Kuonetsera munthu comuyenera;

24. Pamenepo Mulungu amcitira cifundo, nati,Mlanditse, angatsikire kumanda,Ndampezera dipo.

25. Mnofu wace udzakhala se, woposa wa mwana;Adzabwerera ku masiku a ubwana wace.

26. Apembedza Mulungu, ndipo amkomera mtima;M'mwemo aona nkhope yace mokondwera;Ndipo ambwezera munthu cilungamo cace.

Yobu 33