Yobu 31:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ngati ndinaona wina alinkutayika wopanda cobvala,Kapena kuti wosowa alibe copfunda;

20. Ngati zuuno zace sizinandiyamika,Ngati sanapfunda ubweya wa nkhosa zanga;

21. Ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa,Popeza ndinaona thandizo langa kucipata;

22. Libanthuke phewa langa paphalo,Ndi dzanja langa liduke pagwangwa.

23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,

Yobu 31