Yobu 29:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Muja ndinaturuka kumka kucipata kumudzi,Muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,

8. Anyamata anandiona nabisala,Okalamba anandinyamukira, nakhala ciriri,

9. Akalonga anadziletsa kulankhula,Ndi kugwira pakamwa pao;

10. Mau a omveka anali zi,Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.

11. Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.

12. Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula;Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.

Yobu 29