10. Mau a omveka anali zi,Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.
11. Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.
12. Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula;Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.
13. Dalitso la iye akati atayike linandidzera,Ndi mtima wa mkazi wamasiye ndinauyimbitsa mokondwera.