Yobu 23:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yace;Ndasungitsa mau a pakamwa pace koposa lamulo langa langa.

13. Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?Ndi ici cimene moyo wace ucifuna acicita.

14. Pakuti adzacita condiikidwiratu;Ndipo zambiri zotere ziri ndi Iye.

15. Cifukwa cace ndiopsedwa pankhope pace;Ndikalingirira, ndicita mantha ndi Iye.

Yobu 23