12. Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yace;Ndasungitsa mau a pakamwa pace koposa lamulo langa langa.
13. Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?Ndi ici cimene moyo wace ucifuna acicita.
14. Pakuti adzacita condiikidwiratu;Ndipo zambiri zotere ziri ndi Iye.
15. Cifukwa cace ndiopsedwa pankhope pace;Ndikalingirira, ndicita mantha ndi Iye.