Yobu 22:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni;Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?

18. Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino;Koma uphungu wa oipa unditalikira.

19. Olungama aciona nakondwera; Ndi osalakwa awaseka pwepwete,

20. Ndi kuti, Zoonadi, otiukirawo alikhidwa,Ndi zowatsalira, moto unazipsereza.

21. Uzolowerane ndi Iye, nukhale ndi mtendere;Ukatero zokoma zidzakudzera,

22. Landira tsono cilamulo pakamwa pace,Nuwasunge maneno ace mumtimamwako.

Yobu 22