14. Koma adati kwa Mulungu, Ticokereni;Pakuti sitifuna kudziwa njira zanu.
15. Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire?Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?
16. Taonani, zokoma zao siziri m'dzanja lao;(Koma uphungu wa oipa unditalikira.)
17. Ngati nyali za oipa zizimidwa kawiri kawiri?Ngati tsoka lao liwagwera?Ngati Mulungu awagawira zowawa mu mkwiyo wace?