Yobu 21:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma adati kwa Mulungu, Ticokereni;Pakuti sitifuna kudziwa njira zanu.

15. Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire?Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?

16. Taonani, zokoma zao siziri m'dzanja lao;(Koma uphungu wa oipa unditalikira.)

17. Ngati nyali za oipa zizimidwa kawiri kawiri?Ngati tsoka lao liwagwera?Ngati Mulungu awagawira zowawa mu mkwiyo wace?

Yobu 21