7. Koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zace;Iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?
8. Adzauluka ngati loto, osapezekanso;Nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.
9. Diso lidamuonalo silidzamuonanso;Ndi malo ace sadzampenyanso.
10. Ana ace adzapempha aumphawi awakomere mtima;Ndi manja ace adzabweza cuma cace.