Yobu 17:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Anthu oongoka mtima adzadabwa naco,Ndi munthu wosalakwa adzadziutsa kumtsotsa wonyoza Mulunguyo.

9. Koma wolungama asungitsa njira yace,Ndi iye wa manja oyera adzakulabe mumphamvu.

10. Koma bwerani inu nonse, idzani tsono;Pakuti sindipeza mwa inu wanzeru.

11. Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka,Zace zace zomwe za mtima wanga.

12. Zisanduliza usiku ukhale usana;Kuunika kuyandikana ndi mdima.

Yobu 17