Yobu 17:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mzimu wanga watha, masiku anga afafanizika,Kumanda kwandikonzekeratu.

2. Zoonadi, ali nane ondiseka;Ndi diso langa liri cipenyere m'kundiwindula kwao.

3. Mupatse cigwiriro tsono, mundikhalire cikole Inu nokha kwanu;Ndani adzapangana nane kundilipirira?

4. Pakuti mwabisira mtima wao nzeru;Cifukwa cace simudzawakuza.

5. Iye wakupereka mabwenzi ace kuukapolo,M'maso mwa ana ace mudzada.

6. Anandiyesanso nthanthi za anthu;Ndipo ndakhala ngati munthu womthira malobvu pankhope pace.

7. M'diso mwanga mucita cizirezire cifukwa ca cisoni,Ndi ziwalo zanga zonse ziribe cithunzi.

Yobu 17