4. Zedi uyesa cabe mantha,Nucepsa cilingiriro pamaso pa Mulungu.
5. Pakuti pakamwa pako paphunzitsa mphulupulu zako,Nusankha lilime la ocenjerera.
6. Pakamwa pako pakutsutsa, si ine ai.Inde milomo yako ikucitira umboni wakukutsutsa.
7. Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?Kapena unayamba kulengedwa ndiwe, osati mapiri?
8. Kodi unamva uphungu wacinsinsi wa Mulungu?Ndipo unadzikokera nzeru kodi?
9. Udziwa ciani, osacidziwa ife?Uzindikira ciani, cosakhala mwa ife?