4. Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?
5. Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;
6. Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;
7. Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?
8. Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.
9. Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?