Yobu 10:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?

5. Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;

6. Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;

7. Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?

8. Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.

9. Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?

Yobu 10