10. Ndipo Yehova ananenanso kwa Ahazi nati,
11. Udzipemphere wekha cizindikilo ca kwa Yehova Mulungu wako; pempha cam'mwakuya, kapena cam'mwamba.
12. Koma Ahazi anati, Sindipemphai ngakhale kumyesa Yehova.
13. Ndipo iye anati, Mverani inu tsopano, inu a nyumba ya Davide; kodi ndi kanthu kakang'ono kwa inu kutopetsa anthu, kuti inu mutopetsa Mulungu wanga?