11. Zipata zako zidzakhalabe zotseguka, sizidzatsekedwa usana pena usiku, kuti abwere naco kwa iwe cuma ca amitundu, ndi mafumu ao otsogozedwa nao pamodzi.
12. Pakuti mtundu ndi ufumu umene udzakana kukutumikira udzaonongeka; inde mitundu imeneyo idzasakazidwa ndithu.
13. Ulemerero wa Lebano udzafika kwa iwe; mtengo wamlombwa, mtengo wamkuyu ndi mtengo wanaphini pamodzi, kukometsera malo a kacisi wanga; ndipo ndidzacititsa malo a mapazi anga ulemerero.
14. Ndipo ana amuna a iwo amene anabvuta iwe adzafika, nadzakugwadira; ndipo iwo onse amene anakucepetsa iwe adzagwadira ku mapazi ako, nadzakucha iwe, Mudzi wa Yehova, Ziyoni wa Woyera wa Israyeli.