Yesaya 52:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Dzisanse pfumbi; uka, khala tsonga, Yerusalemu; udzimasulire maunyolo a pakhosi pako, iwe mwana wamkazi wam'nsinga wa Ziyoni.

3. Pakuti atero Yehova, Inu munagulitsidwa cabe, ndipo mudzaomboledwa opanda ndalama.

4. Pakuti Ambuye Yehova atero, Anthu anga ananka ku Aigupto poyamba paja, kukakhala kumeneko; ndipo Asuri anawatsendereza popanda cifukwa.

5. Cifukwa cace kodi ndicitenji pano? ati Yehova; popeza anthu anga acotsedwa popanda kanthu? akuwalamulira awaliritsa, ati Yehova; ndipo dzina langa licitidwa mwano tsiku lonse kosalekeza.

6. Cifukwa cace anthu anga adzadziwa dzina langa; cifukwa cacersiku limenelo iwo adzadziwa kuti Ine ndine amene ndinena; taonani, ndine pano.

Yesaya 52