17. Galamuka, galamuka, imirira Yerusalemu amene unamwa m'dzanja la Yehova cikho ca ukali wace; iwe wamwa mbale ya cikho conjenjemeretsa ndi kucigugudiza.
18. Palibenso wina wakumtsogolera mwa ana amuna onse, amene iye anawabala; palibe wina amgwira dzanja mwa ana onse anawalera.
19. Izi ziwiri zakugwera; ndani adzakulira iwe? bwinja ndi cipasuko, njala ndi lupanga; ndidzatonthoza mtima wako bwanji?
20. Ana ako amuna akomoka; agona pamtu pa makwalala onse, monga nswala muukonde; adzala ndi ukali wa Yehova, kudzudzula kwa Mulungu wako,
21. Cifukwa cace imva ici tsopano, iwe wobvutidwa ndi woledzera koma si ndi vinyo ai;