Yesaya 50:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Taonani, Ambuye Yehova adzathandiza Ine; ndani amene adzanditsutsa? taonani, iwo onse adzatha ngati cobvala, njenjete zidzawadya.

10. Ndani ali mwa inu amene amaopa Yehova, amene amamvera mau a mtumiki wace? Iye amene ayenda mumdima, ndipo alibe kuunika, akhulupirire dzina la Yehova, ndi kutsamira Mulungu wace.

11. Taonani, inu nonse amene muyatsa moto, amene mudzimangira m'cuuno ndi nsakali, yendani inu m'cirangati ca moto wanu, ndi pakati pa nsakali zimene mwaziyatsa. Ici mudzakhala naco ca pa dzanja langa; mudzagona pansi ndi cisoni.

Yesaya 50