Yesaya 45:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndadzilumbira ndekha, mau acokera m'kamwa mwanga m'cilungamo, ndipo sadzabwerera, kuti mabondo onse adzandigwadira Ine, malilime onse nadzalumbira Ine.

24. Koma mwa Yehova yekha, wina adzati kwa Ine, muli cilungamo ndi mphamvu; ngakhale kwa Iyeyo anthu adzafika, ndi onse amene anamkwiyira, adzakhala ndi manyazi.

25. Mwa Yehova mbeu yonse ya Israyeli idzalungamitsidwa ndi 7 kudzikuza.

Yesaya 45