21. anthu amene ndinadzilengera ndekha, kuti aonetse matamando anga.
22. Komabe iwe sunandiitane Ine, Yakobo; koma iwe walema ndi Ine, Israyeli.
23. Iwe sunanditengere Ine zoweta zazing'ono za nsembe zopsereza zako; kapena kundilemekeza ndi nsembe zako. Sindinakutumikiritsa ndi nsembe zaufa, kapena kukutopetsa ndi zonunkhira.
24. Iwe sunandigulire Ine nzimbe ndi ndarama, pena kundikhutitsa ndi mafuta a nsembe zako. Koma iwe wanditumikiritsa ndi macimo ako, wanditopetsa ndi mphulupulu zako.