Yesaya 40:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mutonthoze, mutonthoze mtima wa anthu anga, ati Mulungu wanu.

2. Munene inu zotonthoza mtima kwa Yerusalemu, nimupfuulire kwa iye, kuti nkhondo yace yatha, kuti kuipa kwace kwakhululukidwa; kuti iye walandira mowirikiza m'dzanja la Yehova, cifukwa ca macimo ace onse.

3. Mau a wopfuula m'cipululu, Konzani njira ya Yehova, lungamitsani m'dziko loti se khwalala la Mulungu wathu.

Yesaya 40