Yesaya 38:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Masiku amenewo Hezekiya anadwala, nafuna kufa. Ndipo Yesaya mneneri, mwana wa Amozi, anadza kwa iye, nati kwa iye, Atero Yehova, Konza nyumba yako, pakuti iwe udzafa, sudzakhala ndi moyo.

2. Ndipo Hezekiya analoza nkhope yace kukhoma, napemphera kwa Yehova, nati,

3. Kumbukiranitu tsopano, Yehova, kuti ndayenda pamaso panu m'zoonadi ndi mtima wangwiro, ndipo ndacita zabwino pamaso panu. Ndipo Hezekiya analira kolimba.

Yesaya 38