8. Inde, milombwa ikondwera ndi iwe, ndi mikungudza ya Lebano, ndi kunena, Cigwetsere iwe pansi, palibe wokwera kudzatidula ife.
9. Kunsi kwa manda kugwedezeka, cifukwa ca iwe, kukucingamira podza pako; kukuutsira iwe mizimu, ngakhale onse akuru akuru a dziko lapansi; kukweza kucokera m'mipando yao mafumu onse a amitundu.
10. Onse adzabvomera, nadzati kwa iwe, Kodi iwe wakhalanso wopanda mphamvu ngati ife? kodi iwe wafanana nafe?
11. Cifumu cako catsitsidwa kunsi ku manda, ndi phokoso la mingoli yako; mbozi zayalidwa pansi pa iwe, ndi mphukutu zakukuta.
12. Wagwadi kucokera kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mbanda kuca! Wagwetsedwa pansi, iwe wolefula amitundu!