28. Caka cimene mfumu Ahazi anamwalira katundu amene analipo.
29. Usakondwere, lwe Filistia, wonsewe, potyoka ndodo inakumenya; pakuti m'muzu wa njoka mudzaturuka mphiri, ndimo cipatso cace cidzakhala njoka yamoto youluka.
30. Ndi oyamba kubadwa a osauka adzadya, aumphawi nadzagona pansi osatekeseka; ndipo ndidzapha muzu wako ndi njala, ndi otsala ako adzaphedwa.
31. Lira, cipata iwe; pfuula, mudzi iwe; wasungunuka, Filistia wonsewe, pakuti utsi ucokera kumpoto, ndipo palibe wosokera m'mizere yace.
32. Ndipo adzayankhanji amithenga a amitundu? Kuti Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo m'menemo anthu ace obvutidwa adzaona pobisalira.