Yesaya 14:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Iwe sudzaphatikizidwa pamodzi nao poikidwa, pakuti iwe waononga dziko lako, wapha anthu ako; mbeu ya ocita zoipa sidzachulidwa konse.

21. Konzani inu popherapo ana ace, cifukwa ca kuipa kwa atate ao; kuti iwo asadzauka ndi kukhala nalo dziko, ndi kudzaza dziko lapansi ndi midzi.

22. Ndipo Ine ndidzawaukira, ati Yehova wa makamu, ndi kuononga ku Babulo dzina ndi otsala, ndi mwana wamwamuna, ndi cidzukulu cacimuna, ati Yehova.

23. Ndidzayesapo pokhala nungu, ndi madziwe a madzi; ndipo ndidzasesapo ndi tsace la cionongeko, ati Yehova wa makamu.

24. Yehova wa makamu walumbira, nati, Ndithu monga ndaganiza, cotero cidzacitidwa; ndipo monga ndapanga uphungu, cotero cidzakhala;

Yesaya 14