Yesaya 12:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Cifukwa cace mudzakondwera pakutunga madzi m'zitsime za cipulumutso.

4. Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lace, mulalikire macitidwe ace mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lace lakwezedwa.

5. Muyimbire Yehova; pakuti wacita zaulemerero; cidziwike ici m'dziko lonse.

6. Tapfuula, takuwa iwe, wokhala m'Ziyoni, cifukwa Woyera wa Israyeli wa m'kati mwako ali wamkuru.

Yesaya 12