Yesaya 12:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wacoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

2. Taonani, Mulungu ndiye cipulumutso canga; ndidzakhulupira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye cipulumutso canga.

3. Cifukwa cace mudzakondwera pakutunga madzi m'zitsime za cipulumutso.

Yesaya 12