Yeremiya 9:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Nenani, atero Yehova, Mitembo yathu idzagwa ngati ndowe pamunda, ndi monga cipukutu pambuyo pa wakusenga, palibe wocitola.

23. Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zace, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yace, wacuma asadzitamandire m'cuma cace;

24. koma wakudzitamandira adzitamandire adzikweze umo, kuti ali wakuzindikira, ndi kundidziwa Ine, kuti ndine Yehova wakucita zokoma mtima, ciweruziro, ndi cilungamo m'dziko lapansi, pakuti m'menemo ndikondwerera, ati. Yehova.

25. Taonani, masiku alikudza, ati Yehova, kuti ndidzalanga onse odulidwa m'kusadulidwa kwao;

Yeremiya 9