18. Ngwacabe, ciphamaso; nthawi yakulangidwa kwao adzatayika.
19. Gawo la Yakobo silifanafana ndi izo; pakuti Iye ndiye analenga zonse; Israyeli ndi mtundu wa colowa cace, dzina lace ndi Yehova wa makamu.
20. Iwe ndiwe cibonga canga ndi zida zanga za nkhondo; ndi iwe ndidzatyolatyola amitundu, ndi iwe ndidzaononga maufumu;
21. ndi iwe ndidzatyolatyola kavalo ndi wakwera wace;
22. ndi iwe ndidzatyolatyola gareta ndi iye wokweramo; ndi iwe ndidzatyolatyola mwamuna ndi mkazi; ndi iwe ndidzatyolatyola wokalamba ndi mnyamata; ndi iwe ndidzatyolatyola mnyamata ndi namwali;
23. ndi iwe ndidzatyolatyola mbusa ndi zoweta zace; ndi iwe ndidzatyolatyola wakulima ndi gori la ng'ombe lace; ndi iwe ndidzatyolatyola akazembe ndi ziwanga,