Yeremiya 46:24-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Mwana wace wamkazi wa Aigupto adzacitidwa manyazi, adzaperekedwa m'manja a anthu a kumpoto.

25. Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, ati: Taonani, ndidzalanga Amoni wa No, ndi Farao, ndi Aigupto, pamodzi ndi milungu yace, ndi mafumu ace; ngakhale Farao, ndi iwo akumkhulupirira iye;

26. ndipo ndidzawapereka m'manja a iwo amene afuna moyo wao, ndi m'dzanja la Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo, ndi m'manja a atumiki ace; pambuyo pace adzakhalamo anthu, monga masiku akale, ati Yehova.

Yeremiya 46