Yeremiya 37:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo panali pamene nkhondo ya Akasidi inacoka ku Yerusalemu cifukwa ca nkhondo ya Farao,

12. pamenepo Yeremiya anaturuka m'Yerusalemu kumuka ku dziko la Benjamini, kukalandira gawo lace kumeneko.

13. Pokhala iye m'cipinda ca Benjamini, kapitao wa alonda anali kumeneko, dzina lace Iriya, mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya; ndipo iye anamgwira Yeremiya mneneri, nati, Ulinkupandukira kwa Akasidi.

14. Ndipo anati Yeremiya, Kunama kumeneko; ine sindipandukira kwa Akasidi; koma sanamvera iye; ndipo Iriya anamgwira Yeremiya, nanka naye kwa akuru.

Yeremiya 37