Yeremiya 31:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, Kawirinso adzanena mau awa m'dziko la Yuda ndi m'midzi yace, pamene ndibwezanso undende wao; Yehova akudalitse iwe, wokhalamo cilungamo, iwe phiri lopatulika.

24. Ndipo Yuda ndi midzi yace yonse adzakhalamo pamodzi; alimi, ndi okusa zoweta.

25. Pakuti ndakhutidwa mtima wolema, ndadzazanso mtima uli wonse wacisoni.

26. Pamenepo ndinauka, ndinaona; ndipo tulo tanga tinandizunira ine.

27. Taonani, masiku adza, ati Yehova, amene ndidzafesera nyumba ya Israyeli ndi nyumba ya Yuda ndi mbeu ya anthu ndi mbeu ya nyama.

Yeremiya 31