Yeremiya 31:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Nthawi yomweyo, ati Yehova, ndidzakhala Mulungu wa mabanja onse a Israyeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.

2. Atero Yehova, Anthu opulumuka m'lupanga anapeza cisomo m'cipululu; Israyeli, muja anakapuma.

3. Yehova anaonekera kwa ine kale, ndi kuti, Inde, ndakukonda iwe ndi cikondi cosatha; cifukwa cace ndakukoka iwe ndi kukukomera mtima.

4. Ndidzamangitsanso mudzi wako, ndipo udzamangidwa, iwe namwali wa Israyeli; udzakometsedwanso ndi mangaka, ndipo udzaturukira masewero a iwo akukondwerera.

5. Ndiponso udzalima minda ya mphesa pa mapiri a Samariya; akunka adzanka, nadzayesa zipatso zace zosapatulidwa.

Yeremiya 31