Yeremiya 29:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. anatumiza kalatayo m'dzanja la Elasa mwana wace wa Safani, ndi Gemariya mwana wace wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatuma ku Babulo kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo, kuti,

4. Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero, kwa am'nsinga onse, amene ndinawatenga ndende ku Yerusalemu kunka nao ku Babulo:

5. Mangani nyumba, khalani m'menemo; limani minda, idyani zipatso zace;

6. tengani akazi, balani ana amuna ndi akazi; kwatitsani ana anu amuna, patsani ananu akazi kwa amuna, kuti abale ana amuna ndi akazi; kuti mubalane pamenepo, musacepe.

Yeremiya 29