Yeremiya 20:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Muyimbire Yehova, mulemekeze Yehova; pakuti walanditsa moyo wa aumphawi m'dzanja la ocita zoipa.

14. Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa; lisadalitsike tsiku limene amai wanga anandibala ine.

15. Atembereredwe munthu amene anatengera mau kwa atate wanga, kuti, Mwana wamwamuna anakubadwira iwe; ndi kumsekeretsatu iye.

16. Munthuyo akhale ngati midzi imene Yehova anapasula, osalekerera; amve mpfuu mamawa, ndi mkuwo pausana;

Yeremiya 20