Yeremiya 20:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pakuti ndamva kugogodera kwa ambiri, mantha pozungulira ponse. Neneza, ndipo tidzamneneza iye, ati atsamwali anga onse, amene ayang'anira kutsimphina kwanga; kapena adzakopedwa, ndipo ife tidzamlaka iye, ndipo tidzambwezera cilango.

11. Koma Yehova ali ndi ine ngati wamphamvu ndi woopsya; cifukwa cace ondisautsa adzapunthwa, sadzandilala; adzakhala ndi manyazi ambiri, cifukwa sanacita canzeru, ngakhale ndi kunyazitsa kwamuyaya kumene sikudzaiwalika.

12. Koma, Inu Yehova wa makamu, amene muyesa olungama, amene muona imso ndi mtima, mundionetse ine kubwezera cilango kwanu pa iwo; pakuti kwa inu ndaululira mlandu wanga.

Yeremiya 20