Yeremiya 17:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Mtima ndiwo wonyenga koposa, ndi wosaciritsika, ndani angathe kuudziwa?

10. Ine Yehova ndisanthula mtima, ndiyesa imso, kuti ndimpatse munthu yense monga mwa njira zace, monga zipatso za nchito zace.

11. Monga nkhwali iumatira pa mazira amene sinaikira, momwemo iye amene asonkhanitsa cuma, koma mosalungama; pakati pa masiku ace cidzamsiya iye, ndipo pa citsirizo adzakhala wopusa.

Yeremiya 17