15. ndipo pemphero la cikhulupiriro lidzapulumutsa wodwalayo, ndipo Ambuye adzamuukitsa; ndipo ngati adacita macimo adzakhululukidwa kwa iye.
16. Cifukwa cace mubvomerezane wina ndi mnzace macimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzace kuti muciritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukuru m'macitidweace.
17. Eliya anali munthu wakumva zomwezi tizimva ife, ndipo anapemphera cipempherere kuti isabvumbe mvula; ndipo, siinagwa mvula pa dzikozaka zitatu kudza miyezi isanu ndi umodzi.
18. Ndipo anapempheranso; ndipo m'mwamba munatsika mvula, ndi dziko lidabala zipatso zace.