Yakobo 1:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Khalani akucita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

23. Pakuti ngati munthu ali wakumva mau wosati wakucita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yace ya cibadwidwe cace m'kalirole;

24. pakuti wadziyang'anira yekha nacoka, naiwala pompaja nali wotani.

25. Koma iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero cipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakucita nchito, adzakhala wodala m'kucita kwace.

Yakobo 1