Oweruza 6:34-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Koma mzimu wa Yehova unabvana Gideoni; naomba lipenga iye, ndi a banja la Abieziri analalikidwa kumtsata iye.

35. Ndipo anatuma mithenga kwa Manase konse; ndi iwonso analalikidwa kumtsata iye; natuma mithenga kwa Aseri, ndi kwa Zebuloni, ndi kwa Nafitali; iwo nadzakomana nao.

36. Ndipo Gideoni anati kwa Mulungu, Mukadzapulumutsa Israyeli ndi dzanjalanga monga mwanena,

Oweruza 6