Oweruza 6:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja la Midyani zaka zisanu ndi ziwiri.

2. Pamene dzanja la Midyani linalaka Israyeli, ana a Israyeli anadzikonzera ming'ang'ala ya m'mapiri, ndi mapanga, ndi malinga cifukwa ca Midyani.

3. Ndipo kunali, akabzala Israyeli, amakwera Amidyani, ndi Amaleki, ndi ana a kum'mawa, inde amawakwerera;

Oweruza 6