5. Nandiukira eni ace a Gibeya, nandizingira nyumba usiku; nafuna kundipha ine, namcitira coipa mkazi wanga wamng'ono, nafa iye,
6. Pamenepo ndinagwira mkazi wanga wamng'ono ndi kumgawa ndi kumtumiza m'dziko lonse la colowa ca Israyeli, pakuti anacita cocititsa manyazi ndi copusa m'lsrayeli.
7. Taonani, inu nonse, ndinu ana a Israyeli, mudzinenere mau ndi kudzipangira nokha kuno.
8. Ndipo anthu onse anauka ngati munthu mmodzi, ndi kuti, Palibe mmodzi wa ife adzamuka kuhema kwace, kapena kupambukira nyumba yace,
9. koma tsopano ici ndico tidzacitira Gibeya: tidzaukwerera ndi kulota maere.
10. Ndipo tidzatapa amuna khumi limodzi pa zana limodzi, mwa mapfuko onse a Israyeli; ndi zana limodzi pa zikwi cimodzi, ndi cikwi cimodzi pa zikwi khumi kutengera anthu kamba; kuti pakufika ku Gibeya wa Benjamini, aucitire monga mwa copusa conse unacita m'Israyeli.