Oweruza 20:42-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Nabwerera iwo pamaso pa amuna a Israyeli kumka njira ya cipululu; koma nkhondo inawaloodetsa; ndi aja oturuka m'mudzi anawaononga pakati pao.

43. Anawazinga Abenjamini, anawapitikitsa, nawapondereza pampumulo mpaka pandunji pa Gibeya, koturukira dzuwa.

44. Ndipo adagwa a Benjamini amuna zikwi khumi ndi zisanu ndi zitatu; iwo onse ndiwo ngwazi.

45. Natembenuka iwo, nathawira kucipululu ku thanthwe la Rimoni; koma anawakunkha m'makwalala amuna zikwi zisanu; nawalondetsa ku Gidomu, nakantha a iwowa amuna zikwi ziwiri.

Oweruza 20