Oweruza 2:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Cifukwa cacenso ndinati, Sindidzawapitikitsa kuwacotsa pamaso panu; koma adzakhala ngati minga m'nthiti zanu, ndi milungu yao idzakhalira inu msampha.

4. Ndipo kunali, pamene mthenga wa Yehova ananena mau awa kwa ana onse a Israyeli, anthuwo anakweza mau ao, nalira misozi.

5. Potero analicha dzina la malowo Bokimu: namphera Yehova nsembe pomwepo.

6. Pamene Yoswa atawalola anthu amuke, ana a Israyeli anamuka, yense ku colowa cace, dziko likhale lao lao.

7. Ndipo anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a Yoswa ndi masiku onse a akulu akulu otsala atafa Yoswa, amene adaona nchito yaikuru yonse ya Yehova anaicitira Israyeli.

8. Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova anafa wa zaka zace zana ndi khumi.

9. Ndipo anamuika m'malire a colowa cace m'Timinatiheresi, ku mapiri a Efraimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.

10. Ndiponso mbadwo uwu wonse unasonkhanidwa kuikidwa kwa makolo ao; nuuka mbadwo wina pambuyo pao; wosadziwa Yehova kapena nchitoyi adaicitira Israyeli,

Oweruza 2