Oweruza 2:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova, natumikira Abaala;

12. nasiya Yehova Mulungu wa makolo ao, amene adawaturutsa m'dziko la Aigupto, natsata milungu yina, milungu ya mitundu ya anthu okhala pozungulira pao, naigwadira; nautsa mkwiyo wa Yehova.

13. Ndipo anasiya Yehova, natumikira Baala ndi Asitaroti.

14. Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira Israyeli, ndipo anawapereka m'manja a ofunkha kuti awafunkhe; nawagulitsa m'dzanja la adani ao akuwazungulira osakhozanso iwowo kuima pamaso pa adani ao.

15. Kuli konse anaturuka, dzanja la Yehova linawakhalira moipa, monga Yehova adanena, ndi monga Yehova adawalumbirira; nasautsika kwambiri iwowa.

Oweruza 2