Oweruza 2:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndiponso mbadwo uwu wonse unasonkhanidwa kuikidwa kwa makolo ao; nuuka mbadwo wina pambuyo pao; wosadziwa Yehova kapena nchitoyi adaicitira Israyeli,

11. Ndipo ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova, natumikira Abaala;

12. nasiya Yehova Mulungu wa makolo ao, amene adawaturutsa m'dziko la Aigupto, natsata milungu yina, milungu ya mitundu ya anthu okhala pozungulira pao, naigwadira; nautsa mkwiyo wa Yehova.

Oweruza 2