18. Ndipo pamene Delila anaona kuti adamfotokozera mtima wace wonse, anatuma naitana akalonga a Afilisti, ndi kuti, Kwerani nthawi yino, pakuti wandifotokozera za mtima wace wonse. Nakwera akalonga a Afilisti nadza kwa iye nabwera nazo ndalamazo m'dzanja lao.
19. Pamenepo anamgonetsa pa mabondo ace, naitana munthu, nameta njombi zace zisanu ndi ziwiri; nayamba kumzunza, nimcokera mphamvu yaceo
20. Ndipo anati, Afilisti akugwera, Samsoni. Nagalamuka iye m'tulo tace, nati, Ndizituruka ngati nthawi zina, ndi kudzitakasika. Koma sanadziwa kuti Yehova adamcokera.
21. Pamenepo Afilisti anamgwira, namkolowola maso, natsika naye ku Gaza, nammanga ndi maunyolo amkuwa; namperetsa m'kaidi.
22. Koma atammeta tsitsi la pamutu pace linayamba kumeranso.