Nyimbo 8:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndine khoma, maere anga akunga nsanja zace:Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.

11. Solomo anali ndi munda wamipesa ku Baalahamoni;Nabwereka alimi mundawo;Yense ambwezere ndalama cikwi cifukwa ca zipatso zace.

12. Koma munda wanga wamipesa, uli pamaso panga ndiwo wangatu;Naco cikwico, Solomo iwe,Koma olima zipatso zace azilandira mazana awiri.

13. Namwaliwe wokhala m'minda,Anzake amvera mau ako:Nanenso undimvetse.

14. Dzifulumira, mnyamatawe wokondedwa wanga,Dzifanane ngati mphoyo pena mwana wa mbawalaPa mapiri a mphoka,

Nyimbo 8