Nyimbo 7:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,Ndine amene andifunayo.

11. Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda;Titsotse m'miraga.

12. Tilawire kunka ku minda yamipesa;Tiyang'ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso,Makangaza ndi kutuwa maluwa ace;Pompo ndidzakupatsa cikondi canga,

13. Mandimu anunkhira,Ndi pamakomo pathu zipatso zabwino, za mitundu mitundu, zakale ndi zatsopano,Zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.

Nyimbo 7