Nyimbo 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndalowa m'munda mwanga, mlongwanga, mkwatibwi:Ndachera nipa yanga ndi zonunkhiritsa zanga;Ndadya uci wanga ndi cisa cace;Ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.Idyani, atsamwalinu,Imwani, mwetsani cikondi.

2. Ndinagona tulo, koma mtima wanga unali maso:Ndi mau a bwenzi langa mnyamatayo agogoda, nati,Nditsegulire, mlongwanga, wokondedwa wanga, nkhunda yanga, wangwiro wanga:Pakuti pamtu panga padzala mame,Patsitsi panga pali madontho a usiku.

3. Ndinayankha kuti, Ndabvula maraya anga, ndiwabvalenso bwanji?Ndatsuka mapazi anga; ndiwadetserenii?

Nyimbo 5